Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 15:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo anati, Ambuye Mulungu, nanga ndidzadziwa bwanji kuti lidzakhala colowa canga?

9. Ndipo anati kwa iye, Kanditengere Ine ng'ombe yaikazi ya zaka zitatu, ndi mbuzi yaikazi ya zaka zitatu, ndi tonde wa zaka zitatu, ndi njiwa, ndi bunda.

10. Ndipo anatenga iye zonse zimenezo, nazidula pakati, naika bandu popenyana ndi linzace: koma mbalame sanazidula.

11. Pamene miimba inatsikira panyama, Abramu anaingitsa iyo.

12. Ndipo linalinkulowa dzuwa, ndi tulo tatikuru tinamgwera Abramu: ndipo taonani, kuopsya kwa mdima waukuru kunamgwera iye.

13. Ndipo anati kwa Abramu, Dziwitsa ndithu kuti mbeu zako zidzakhala alendo m'dziko la eni, nizidzatumikira iwo, ndipo iwo adzasautsa izo zaka mazana anai;

Werengani mutu wathunthu Genesis 15