Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 11:14-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo Sela anakhala ndi moyo zaka makumi atatu, nabala Ebere;

15. ndipo Sela anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza zitatu, atabala Ebere, nabala ana amuna ndi akazi.

16. Ndipo Ebere anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza zinai, nabala Pelege;

17. ndipo Ebere anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza makumi awiri, atabala Pelege, nabala ana amuna ndi akazi.

18. Ndipo Pelege anakhala ndi moyo zaka makumi atatu, nabala, Reu;

19. ndipo Pelege anakhala ndi moyo zaka mazana awiri kudza zisanu ndi zinai, atabala Reu, nabala ana amuna ndi akazi.

20. Ndipo Reu anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza ziwiri, nabala Serugi:

21. ndipo Reu anakhala ndi moyo zaka mazana awiri kudza zisanu ndi ziwiri, atabala Serugi, nabala ana amuna ndi akazi.

Werengani mutu wathunthu Genesis 11