Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 11:10-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Mibadwo ya Semu ndi iyi: Semu anali wa zaka zana limodzi ndipo anabala Aripakasadi, citapita cigumula zaka ziwiri;

11. ndipo Semu anakhala ndi moyo zaka mazana asanu, atabala Aripakasadi, nabala ana amuna ndi akazi.

12. Ndipo Aripakasadi anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza zisanu, nabala Sela;

13. ndipo Aripakasadi anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza zitatu, atabala Sela, nabala ana amuna ndi akazi.

14. Ndipo Sela anakhala ndi moyo zaka makumi atatu, nabala Ebere;

15. ndipo Sela anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza zitatu, atabala Ebere, nabala ana amuna ndi akazi.

16. Ndipo Ebere anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza zinai, nabala Pelege;

17. ndipo Ebere anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza makumi awiri, atabala Pelege, nabala ana amuna ndi akazi.

18. Ndipo Pelege anakhala ndi moyo zaka makumi atatu, nabala, Reu;

19. ndipo Pelege anakhala ndi moyo zaka mazana awiri kudza zisanu ndi zinai, atabala Reu, nabala ana amuna ndi akazi.

20. Ndipo Reu anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza ziwiri, nabala Serugi:

Werengani mutu wathunthu Genesis 11