Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 10:21-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndiponso kwa Semu atate wa ana onse a Ebere, mkuru wa Yafeti, kwa iye kunabadwa ana.

22. Ana amuna a Semu; Elamu, ndi Ashuri, ndi Aripakasadi, ndi Ludi, ndi Aramu.

23. Ndi ana a Aramu: Uzi ndi Huli, ndi Getere, ndi Masi.

24. Aripakasadi ndipo anabala Sela; ndipo Sela anabala Ebere.

25. Kwa Ebere ndipo kunabadwa ana amuna awiri; dzina la wina ndi Pelege; cifukwa kuti m'masiku ace dziko lapansi linagawanikana; dzina la mphwace ndi Yokitani.

26. Ndipo Yokitani anabala Alamodadi, ndi Selefe, ndi Hazaramaveti, ndi Yera;

27. ndi Hadorimu ndi Uzali, ndi Dikila;

28. ndi Obali, ndi Abimaele, ndi Sheva;

29. ndi Ofiri ndi Havila, ndi obabi; onse amenewa ndi ana a okitani.

30. Kwao kunayamba pa Mesa pakunka ku Sefere phiri la kum'mawa.

31. Amenewa ndi ana a Semu, monga mwa mabanja ao, mwa zinenedwe zao, m'maiko ao, m'mitundu yao.

32. Amenewo ndi mabanja a ana a Nowa monga mwa mibadwo yao, m'mitundu yao: ndi amenewo anagawanika mitundu pa dziko lapansi, citapita cigumula.

Werengani mutu wathunthu Genesis 10