Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 10:19-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo malire a Akanani anayamba pa Sidoni, pakunka ku Gerari ndi ku Gaza; pakunka ku Sodomu, ndi ku Gomora, ndi Adima, ndi Zeboimu, kufikira ku Lasa.

20. Amenewa ndi ana amuna a Hamu monga mwa mabanja ao, mwa zinenedwe zao, m'maiko ao, m'mitundu yao.

21. Ndiponso kwa Semu atate wa ana onse a Ebere, mkuru wa Yafeti, kwa iye kunabadwa ana.

22. Ana amuna a Semu; Elamu, ndi Ashuri, ndi Aripakasadi, ndi Ludi, ndi Aramu.

23. Ndi ana a Aramu: Uzi ndi Huli, ndi Getere, ndi Masi.

24. Aripakasadi ndipo anabala Sela; ndipo Sela anabala Ebere.

25. Kwa Ebere ndipo kunabadwa ana amuna awiri; dzina la wina ndi Pelege; cifukwa kuti m'masiku ace dziko lapansi linagawanikana; dzina la mphwace ndi Yokitani.

26. Ndipo Yokitani anabala Alamodadi, ndi Selefe, ndi Hazaramaveti, ndi Yera;

27. ndi Hadorimu ndi Uzali, ndi Dikila;

Werengani mutu wathunthu Genesis 10