13. Mizraimu ndipo anabala Ludimu, ndi Anamimu, ndi Lehabimu, ndi Nafituhimu,
14. ndi Patrusimu, ndi Kasiluhimu, m'menemo ndipo anaturuka Afilisti, ndi Kafitorimu.
15. Ndipo Kanani anabala Sidoni woyamba wace, ndi Heti:
16. ndi Ajebusi, ndi Aamori, ndi Agirigasi;
17. ndi Ahivi, ndi Aariki, ndi Asini;
18. ndi Aaravadi, ndi Aazemari, ndi Ahamati; pambuyo pace pamenepo ndipo mabanja a Akanani anafalikira.
19. Ndipo malire a Akanani anayamba pa Sidoni, pakunka ku Gerari ndi ku Gaza; pakunka ku Sodomu, ndi ku Gomora, ndi Adima, ndi Zeboimu, kufikira ku Lasa.
20. Amenewa ndi ana amuna a Hamu monga mwa mabanja ao, mwa zinenedwe zao, m'maiko ao, m'mitundu yao.
21. Ndiponso kwa Semu atate wa ana onse a Ebere, mkuru wa Yafeti, kwa iye kunabadwa ana.
22. Ana amuna a Semu; Elamu, ndi Ashuri, ndi Aripakasadi, ndi Ludi, ndi Aramu.