7. Ndipo anadza nane ku cipata ca kubwalo, ndipo popenya ine, taonani, pobooka palinga.
8. Pamenepo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, booletsa kulinga; ndipo nditabooletsa palinga, ndinaona khomo.
9. Ndipo anati kwa ine, Lowa, kapenye zonyansa zoipa alikuzicita komweko.