Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 48:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Maina a mafuko tsono ndi awa: Kuyambira nsonga ya kumpoto, ku mbali ya njira ya ku Heteloni, polowera ku Hamati, Hazarenani ku malire a Damasiko kumpoto, ku mbali ya ku Hamati; ndi mbali zace zilinge kum'mawa ndi kumadzulo; Dani akhale nalo gawo limodzi.

2. Ndi m'malire a Dani, kuyambira mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Aseri, limodzi.

3. Ndi m'malire a Aseri, kuyambira mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Nafitali, limodzi.

4. Ndi m'malire a Nafitali, kuyambira mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Manase, limodzi.

5. Ndi m'malire a Manase, kuyambira mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Efraimu, limodzi.

6. Ndi m'malire a Efraimu, kuyambira mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Rubeni, limodzi.

7. Ndi m'malire a Rubeni, kuyambira mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Yuda, limodzi.

8. Ndi m'malire a Yuda, kuyambira mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo, pakhale copereka a mucipereke, mabango zikwi makumi awiri mphambu zisanu kupingasa kwace, ndi m'litali mwace lilingane ndi magawo enawo, kuyambira mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo; ndi malo opatulika akhale pakati pace.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 48