Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 47:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndi mbali ya kumwela kuloza kumwela ndiyo kuyambira ku Tamara kufikira ku madzi a Meriboti Kadesi, ku mtsinje wa Aigupto, ndi ku nyanja yaikuru. Ndiyo mbali ya kumwela kuloza kumwela.

20. Ndi mbali ya kumadzulo ndiyo nyanja yaikuru, kuyambira malire a kumwela kufikira pandunji polowera ku Hamati. Ndiyo mbali ya kumadzulo.

21. Motero mudzigawire dziko ili monga mwa mafuko a Israyeli.

22. Ndipo kudzacitika kuti muligawe ndi kucita maere, likhale colowa canu, ndi ca alendo akukhala pakati pa inu; ndipo akhale kwa inu ngati obadwa m'dziko mwa ana a Israyeli, alandire colowa pamodzi ndi inu mwa mafuko a Israyeli.

23. Ndipo kudzatero kuti kupfuko kumene mlendo akhalako kumeneko mumpatse colowa cace, ati Ambuye Yehova.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 47