Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 38:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Perisiya, Kusi, ndi Puti pamodzi nao, onsewo ndi cikopa ndi cisoti cacitsulo;

6. Gomeri ndi magulu ace onse, nyumba ya Togarima, ku malekezero a kumpoto, ndi magulu ace onse, mitundu yambiri pamodzi ndi iwe.

7. Ukonzekeretu, Inde udzikonzeretu, iwe ndi msonkhano wako wonse unakusonkhanira, nukhale iwe mtsogoleri wao.

8. Atapita masiku ambiri udzakumbukirika; zaka zotsiriza udzalowa m'dziko lobwezedwa lopulumuka lupanga, losonkhanidwa lituruke m'mitundu yambiri ya anthu, pa mapiri a Israyeli, amene adakhala acipululu cikhalire; koma liturutsidwa m'mitundu ya anthu, ndipo adzakhala mosatekeseka onsewo.

9. Ndipo udzakwera udzadza ngati mkuntho, udzanga mtambo kuphimba dziko, iwe ndi magulu ako onse, ndi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 38