1. Dzanja la Yehova linandikhalira, ndipo anaturuka nane mu mzimu wa Yehova, nandiika m'kati mwa cigwa, ndico codzala ndi mafupa;
2. ndipo anandipititsa pamenepo pozungulira ponse, ndipo taonani, anali aunyinji pacigwa pansi, ndipo anaumitsitsa.
3. Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, mafupa awa nkukhala ndi moyo kodi? Ndipo ndinati, Ambuye Yehova, mudziwa ndinu.
4. Pamenepo anati kwa ine, Nenera kwa mafupa awa, nuti nao, Mafupa ouma inu, imvani mau a Yehova.
5. Atero Ambuye Yehova kwa mafupa awa, Taonani, ndidzalonga mpweya mwa inu, ndipo mudzakhala ndi moyo.