37. Atero Ambuye Yehova, Ici comwe adzandipempha a nyumba ya Israyeli ndiwacitire ici, ndidzawacurukitsira anthu ngati nkhosa.
38. Ngati nkhosa za nsembe, ngati nkhosa za ku Yerusalemu pa madyerero ace oikika, momwemo midzi yamabwinja idzadzala nao magulu a anthu; motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.