Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 35:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Nandidzeranso mau a Yehova, akuti,

2. Wobadwa ndi munthu iwe, Lozetsa nkhope yako ku phiri la Seiri, nulinenere molitsutsa;

3. nuti nalo, Atero Ambuye Yehova, Taona, ndiipidwa nawe phiri la Seiri, ndipo ndidzakutambasulira dzanja langa, ndi kukusanduliza lacipululu ndi lodabwitsa.

4. Ndidzapasula midzi yako, nudzakhala lacipululu; ndipo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

5. Popeza uli nao udani wosatha, waperekanso ana a Israyeli ku mphamvu ya lupanga m'nthawi ya tsoka lao, mu nthawi ya mphulupulu yotsiriza;

6. cifukwa cace, Pali Ine, ati Ambuye Yehova, ndikukonzeratu uphedwe, ndi mwazi udzakulondola; popeza sunadana nao mwazi, mwazi udzakulondola.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 35