Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 32:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo ndidzaika nyama yako pamapiri, ndi kudzaza zigwa ndi msinkhu wako.

6. Ndipo ndidzamwetsa dziko losambiramo iwe ndi mwazi wako, kufikira kumapiri; ndi mitsinje idzadzala nawe.

7. Ndipo pakukuzima iwe ndidzaphimba thambo, ndi kudetsa nye nyezi zace; ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndi mwezi sudzaonetsa kuwala kwace.

8. Ndidzakudetsera miyuni ronse yakuunikira kuthambo, ndi kucititsa mdima pa dziko lako, ati Ambuye Yehova.

9. Ndidzabvutanso mitima ya mitundu yambiri ya anthu, pakufikitsa Ine cionongeko cako mwa amitundu, m'maiko amene sunawadziwa.

10. Ndipo ndidzasumwitsa nawe mitundu yambiri ya anthu, ndi mafumu ao adzacita malunga cifukwa ca iwe, pakung'animitsa Ine lupanga langa pamaso pao; ndipo adzanjenjemera mphindi zonse, yense cifukwa ca moyo wace tsiku lakugwa Iwe,

11. Pakuti atero Ambuye Yehova, Lupanga la mfumu ya ku Babulo lidzakudzera.

12. Ndidzagwetsa aunyinji ako ndi malupanga a eni mphamvu, ndiwo onse oopsetsa a amitundu; ndipo adzaipsa kudzikuza kwa Aigupto, ndi aunyinji ace onse adzaonongeka.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 32