Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 3:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, Muka, nufike kwa nyumba ya Israyeli, nunene nao mau anga.

5. Pakuti sutumizidwa kwa anthu a cinenedwe cosamveka ndi cobvuta, koma kwa nyumba ya Israyeli;

6. si kwa mitundu yambiri ya anthu a cinenedwe cosamveka ndi cobvuta, amene sukhoza kudziwitsa cinenedwe cao. Zedi ndikakutumiza kwa iwowa adzamvera iwe.

7. Koma nyumba ya Israyeli siidzakumvera, pakuti siifuna kundimvera Ine; pakuti nyumba yonse ya Israyeli ndiyo yolimba mutu ndi youma mtima.

8. Taona ndakhwimitsa nkhope yako itsutsane nazo nkhope zao; ndalimbitsanso mutu wako utsutsane nayo mitu yao.

9. Ndalimbitsa mutu wako woposa mwala wolimbitsitsa, usawaopa kapena kutenga nkhawa pamaso pao; pakuti iwo ndiwo nyumba yopanduka.

10. Ananenanso nane, Wobadwa ndi munthu iwe, mau anga onse ndidzawanena ndi iwe uwalandire m'mtima mwako, utawamva m'makutu mwako.

11. Numuke, nufike kwa andende kwa ana a anthu a mtundu wako, nunene nao ndi kuwauza, Atero Yehova Mulungu, ngakhale akamva kapena akaleka kumva.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 3