25. Atero Ambuye Yehova, Pakusonkhanitsa nyumba ya Israyeli mwa mitundu ya anthu anabalalikamo, ndidzazindikirika Woyera mwa iwowa, pamaso pa amitundu; ndipo adzakhala m'dziko mwao mwao ndinalipereka kwa Yakobo mtumiki wanga.
26. Nadzakhalamo osatekeseka, nadzamanga nyumba, ndi kunka mpesa m'mindamo, nadzakhalamo mosatekeseka, ndikatha kukwaniritsira maweruzo pa onse akuwapeputsa pozungulira pao; motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wao.