Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 26:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Pamenepo zisumbu zidzanjenjemera tsiku la kugwa kwako, inde zisumbu za kunyanja zidzatenga nkhawa pa kucokera kwako.

19. Pakuti atero Ambuye Yehova, Pamene ndikusandutsa mudzi wapasuka, ngati midzi yosakhalamo anthu, ndi kukukweretsera nyanja, nadzakumiza madzi akuru;

20. pamenepo ndidzakutsitsa nao otsikira kumanda, kwa anthu a kale lomwe, ndi kukukhalitsa ku malo a kunsi kwa dziko, kopasukira kale lomwe, pamodzi nao otsikira kumanda, kuti mwa iwe musakhale anthu; ndipo ndidzaika ulemerero m'dziko la amoyo,

21. ndidzakuika woopsa; ndipo sudzaonekanso, cinkana akufunafuna sudzapezekanso konse, ati Ambuye Yehova.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 26