Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 23:33-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Udzadzala ndi kuledzera ndi cisoni, ndi cikho codabwitsa ndi ca cipasuko, ndi cikho ca mkuru wako Samariya.

34. Udzamwa ici ndi kugugudiza, ndi kuceceta-ceceta zibade zace, ndi kung'amba maere ako; pakuti ndacinena, ati Ambuye Yehova.

35. Cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Popeza wandiiwala Ine, ndi kunditaya pambuyo pako, uzisenza iwenso coipa cako ndi zigololo zako.

36. Ndipo Yehova anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? uwafotokozere tsono zonyansa zao.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 23