Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 22:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo ndidzakumwaza mwa amitundu, ndi kukubalalitsa m'maiko, ndi kukuthera zodetsa zako zikucokere.

16. Ndipo udzaipsidwa mwa iwe wekha pamaso pa amitundu; motero udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

17. Ndipo mau a Yehova anandidzera, akuti,

18. Wobadwa ndi munthu iwe, nyumba ya Israyeli yandikhalira mphala; onsewo ndiwo mkuwa, ndi seta, ndi citsulo, ndi ntobvu, m'kati mwa ng'anjo; ndiwo mphala zasiliva.

19. Cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Popeza mwasanduka mphala nonsenu, cifukwa cace taonani, ndidzakusonkhanitsani m'kati mwa Yerusalemu.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 22