Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 20:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali caka cacisanu ndi ciwiri, mwezi wacisanu; tsiku lakhumi la mwezi, anadza akulu ena a Israyeli kufunsira kwa Yehova, nakhala pansi iwowa pamaso panga.

2. Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

3. Wobadwa ndi munthu iwe, lankhula ndi akulu a Israyeli, nunene nao, Atero Ambuye Yehova, Mwadza kodi kufunsira kwa Ine? Pali Ine, sindidzafunsidwa ndi inu, ati Ambuye Yehova.

4. Udzawaweruza kodi, wobadwa ndi munthu iwe? udzawaweruza? uwadziwitse zonyansa za makolo ao,

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 20