Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 18:4-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Taonani, miyoyo yonse ndi yanga, monga moyo wa atate momwemonso moyo wa mwana, ndiyo yanga; moyo wocimwawo ndiwo udzafa.

5. Koma munthu akakhala wolungama, nakacita ciweruzo ndi cilungamo,

6. wosadya pamapiripo, wosakweza maso ace ku mafano a nyumba ya Israyeli, wosaipsa mkazi wa mnansi wace, kapena kuyandikira mkazi ataoloka,

7. wosasautsa munthu ali yense, koma wambwezera wangongole cigwiriro cace, wosatenga zofunkha, anampatsa wanjala cakudya cace, nabveka wamarisece ndi cobvala,

8. wosapereka molira phindu, wosatenga coonjezerapo wobweza dzanja lace lisacite cosalungama, woweruza zoona pakati pa munthu ndi mnzace,

9. amayenda m'malemba anga, nasunga maweruzo anga kucita cokhulupirika; iye ndiye wolungama, adzakhala ndi moyo ndithu, anena Ambuye Yehova.

10. Akabala mwana ndiye mkhungu, wokhetsa mwazi, wocita cimodzi ca izi,

11. wosacita zabwino zonse zija, koma anadyanso pamapiri, naipsa mkazi wa mnansi wace,

12. nasautsa osauka ndi osowa, natenga zofunkha, wosabwezera cigwiriro, nakweza maso ace kumafano, nacita conyansa,

13. napereka molira phindu, nalandira coonjezerapo; adzakhala ndi moyo uyu kodi? sadzakhala ndi moyo, anacita zonyansa izi zonse; kufa adzafadi, niwazi wace umkhalira.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 18