Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 16:56-63 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

56. Ndipo sunakamba za mbale wako Sodomu pakamwa pako tsiku la kudzikuza kwako;

57. cisanabvundukuke coipa cako monga nthawi ya citonzo ca ana akazi a Aramu, ndi onse akumzungulira iye, ana akazi a Afilisti akupeputsa pozungulira ponse.

58. Wasenza coipa cako ndi zonyansa zako, ati Yehova.

59. Pakuti atero Ambuye Yehova, Ndidzacita ndi iwe monga umo unacitira; popeza wapepula lumbiro ndi kutyola pangano.

60. Koma ndidzakumbukila Ine pangano langa ndi iwe m'masiku a ubwana wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha nawe.

61. Pamenepo udzakumbukila njira zako ndi kucita manyazi, pakulandira abale ako akuru ndi ang'ono; ndipo ndidzakupatsa awa akhale ana ako akazi, angakhale sali a pangano lako.

62. Pakuti ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova;

63. kuti uzikumbukila ndi kucita manyazi ndi kusatsegulanso pakamwa pako konse, cifukwa ca manyazi ako, pamene ndikufafanima zonse unazicita, ati Ambuye Yehova.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 16