Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 16:27-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Taona tsono, ndakutambasulira dzanja langa, ndi kucepsa gawo lako la cakudya, ndi kukupereka ku cifuniro ca iwo akudana nawe, kwa ana akazi a Afilisti akucita manyazi ndi njira yako yoipa.

28. Unacitanso cigololo ndi Aasuri, pakuti unakhala wosakoledwa, inde unacita cigololo nao, koma sunakoledwa.

29. Unacurukitsanso cigololo cako m'dziko la Kanani, mpaka dziko la Akasidi, koma sunakoledwa naconso.

30. Ha! mtima wako ngwofoka, ati Ambuye Yehova, pakucita iwe izi zonse, ndizo nchito za mkazi wacigololo wouma m'maso.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 16