Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 16:15-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Koma unatama kukongola kwako, ndi kucita zacigololo potama mbiri yako, ndi kutsanulira zigololo zako pa munthu ali yense wopitapo; unali wace.

16. Ndipo unatengako zobvala zako, ndi kudzimangira misanje ya mawanga mawanga, ndi kucitapo cigololo; zotere sizinayenera kufika kapena kucitika.

17. Unatenganso zokometsera zako zokoma za golidi wanga ndi siliva wanga, zimene ndinakupatsa, ndi kudzipangira mafano a amuna, ndi kucita nao cigololo.

18. Unatenganso zobvala zako za nsaru yopikapika, ndi kuwabveka nazo, unaikanso mafuta anga ndi cofukiza canga pamaso pao.

19. Ndi mkate wanga ndinakupatsawo, ufa wosalala, ndi mafuta, ndi uci, ndinakudyetsazo, unawaikira izi pamaso pao, zicite pfungo lokoma; kunatero, ati Ambuye Yehova.

20. Unatenganso ana ako amuna ndi akazi amene unandibalirawo, ndi kuwapereka nsembe awathe. Zigololo zako zidacepa kodi,

21. kuti unawapha ana anga ndi kuwapereka, pakuwapititsa pamoto?

22. Ndipo pa zonyansa zako zonse ndi zigololo zako sunakumbukila masiku a ubwana wako, mujaunakhala wamarisece ndi wausiwa, wobvimvinizika m'mwazi wako.

23. Ndipo kudacitika utatha zoipa zako zonse, (tsoka iwe, tsoka, ati Ambuye Yehova)

24. unadzimangira nyumba yacimphuli, unadzimangiranso ciunda m'makwalala ali onse.

25. Unamanga ciunda cako pa mphambano ziri zonse, ndipo unanyansitsa kukongola kwako, ndi kutukula mapazi ako kwa yense wopitako, ndi kucurukitsa cigololo cako.

26. Wacitanso cigololo ndi Aaigupto oyandikizana nawe, akulu thupi, ndi kucurukitsa cigololo cako kuutsa mkwiyo wanga.

27. Taona tsono, ndakutambasulira dzanja langa, ndi kucepsa gawo lako la cakudya, ndi kukupereka ku cifuniro ca iwo akudana nawe, kwa ana akazi a Afilisti akucita manyazi ndi njira yako yoipa.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 16