Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 10:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo ulemerero wa Yehova unacoka pa ciundo ca nyumba, nuima pamwamba pa akeruibi.

19. Ndipo akerubi anatambasula mapiko ao, nauluka padziko, ndiri cipenyere, pakucoka iwo ndi njingazi pa mbali pao; ndipo anaima pa citseko ca cipata ca kum'mawa ca nyumba ya Yehova, ndi ulemerero wa Mulungu wa Israyeli unali pamwamba pao.

20. Awa ndi zamoyozo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israyeli kumtsinje Kebara, ndipo ndinadziwa kuti ndiwo akerubi.

21. Yense anali nazo nkhope zinai, ndi yense mapiko anai, ndi cifaniziro ca manja a munthu pansi pa mapiko ao.

22. Ndi cifaniziro ca nkhope zao ndico nkhope zomwezo ndinaziona kumtsinje Kebara, maonekedwe ao ndi iwo eni; ali yense anayenda, nalunjika m'tsogolo.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 10