Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 10:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Pamenepo akerubi anakwera, ndizo zamoyo zija ndinaziona kumtsinje Kebara.

16. Ndipo pakuyenda akerubi, njinga zinayenda pambali pao, ndi pakutambasula mapiko ao akerubiwo kuuluka padziko, njingazi sizinatembenuka pambali pao.

17. Pakuima iwo zinaima izi, ndi pakukwera iwo izi zinakwera pamodzi nao; pakuti mzimu wa zamoyozo unali mwa izo.

18. Ndipo ulemerero wa Yehova unacoka pa ciundo ca nyumba, nuima pamwamba pa akeruibi.

19. Ndipo akerubi anatambasula mapiko ao, nauluka padziko, ndiri cipenyere, pakucoka iwo ndi njingazi pa mbali pao; ndipo anaima pa citseko ca cipata ca kum'mawa ca nyumba ya Yehova, ndi ulemerero wa Mulungu wa Israyeli unali pamwamba pao.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 10