Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 10:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo thupi lao lonse, ndi misana yao, ndi manja ao, ndi mapiko ao, ndi njinga zomwe, zinadzala ndi maso pozungulira pao, zingakhale njingazi anai aja anali nazo.

13. Kunena za njingazi, wina anazipfuulira, ndiri cimvere ine, Kunkhulirani.

14. Ndipo ali yense anali nazo nkhope zinai, nkhope yoyamba ndiyo nkhope ya kerubi, ndi nkhope yaciwiri ndiyo nkhope ya munthu, ndi yacitatu ndiyo nkhope ya mkango, ndi yacinai ndiyo nkhope ya ciombankhanga.

15. Pamenepo akerubi anakwera, ndizo zamoyo zija ndinaziona kumtsinje Kebara.

16. Ndipo pakuyenda akerubi, njinga zinayenda pambali pao, ndi pakutambasula mapiko ao akerubiwo kuuluka padziko, njingazi sizinatembenuka pambali pao.

17. Pakuima iwo zinaima izi, ndi pakukwera iwo izi zinakwera pamodzi nao; pakuti mzimu wa zamoyozo unali mwa izo.

18. Ndipo ulemerero wa Yehova unacoka pa ciundo ca nyumba, nuima pamwamba pa akeruibi.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 10