Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 4:22-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Cenjerani mungadodomepo, cidzakuliranji cisauko ca kusowetsa mafumu?

23. Pamenepo atawerenga malemba a kalata wa mfumu kwa Rehumu, ndi Simsai mlembi, ndi anzao, anafulumira kupita ku Yerusalemu kwa Ayuda, nawaletsa ndi dzanja lamphamvu.

24. Momwemo inalekeka nchito ya nyumba ya Mulungu yokhala ku Yerusalemu; nilekeka mpaka caka caciwiri ca ufumu wa Dariyo mfumu ya Perisiya.

Werengani mutu wathunthu Ezara 4