Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 2:47-65 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

47. ana a Gideli, ana a Gahari, ana a Reaya,

48. ana a Rezini, ana a Nekoda, ana a Gazamu,

49. ana a Uza, ana a Paseya, ana a Besai,

50. ana a Asina, ana a Mehunimu, ana a Nefusimu,

51. ana a Bakabuku, ana a Hakufa, ana a Haruri,

52. ana a Baziluti, ana a Mehida, ana a Harisa,

53. ana a Barikosi, ana a Siseri, ana a Tama,

54. ana a Neziya, ana a Hatifa.

55. Ana a akapolo a Solomo: ana a Sotai, ana a Sofereti, ana a Peruda,

56. ana a Yaala, ana a Darikoni, ana a Gideli,

57. ana a Sefatiya, ana a Hatili, ana a Pokereti wa Zebaimu, ana a Ami.

58. Anetini onse, ndi ana a akapolo a Solomo, ndiwo mazana atatu mphambu makumi asanu ndi anai kudza awiri.

59. Ndipo okwera kucokera ku Telemela, Teleharisa, Kerubi, Adana, Imeri, ndi awa, koma sanakhoza kuchula nyumba za makolo ao ndi mbumba zao ngati ali Aisrayeli:

60. ana a Delaya, ana a Tobiya, ana a Nekoda, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.

61. Ndi ana a ansembe: ana a Habaya, ana a Kozi, ana a Barizilai, amene anadzitengera mkazi wa ana akazi a Barizilai Mgileadi, nachedwa dzina lao.

62. Awa anafunafuna maina ao m'buku la iwo owerengedwa mwa cibadwidwe cao, koma osawapeza; potero anacotsedwa ku nchito ya nsembe monga odetsedwa.

63. Ndipo kazembe anawauza kuti asadyeko zopatulikitsa, mpaka adzabuka wansembe wokhala ndi Urimu ndi Tumimu.

64. Msonkhano wonse pamodzi ndiwo wa zikwi makumi anai ndi awiri mphambu mazana atatu kudza makumi asanu ndi limodzi,

65. osawerenga akapolo ao amuna ndi akazi, ndiwo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu mazana atatu ndi makumi atatu kudza asanu ndi awiri; ndipo anakhala nao amuna ndi akazi oyimbira mazana awiri.

Werengani mutu wathunthu Ezara 2