23. Anthu a ku Anatoti, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.
24. Ana a Azimaveti, makumi anai mphambu awiri.
25. Ana a Kiriyati Arimu, Kefira, ndi Beeroti, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi anai kudza atatu.
26. Ana a Rama ndi Gaba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.
27. Anthu a Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.
28. Anthu a ku Beteli ndi Ai, mazana awiri mphambu makumi awiri kudza atatu.
29. Ana a Nebo, makumi asanu mphambu awiri.
30. Ana a Magabisi, zana limodzi mphambu makumi asanu kudza asanu ndi mmodzi.
31. Ana a Elamu wina, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi asanu ndi anai.
32. Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.
33. Ana a Lodi, Hadidi, ndi Ono, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi awiri kudza asanu.
34. Ana a Yeriko, mazana atatu mphambu makumi anai kudza asanu.
35. Ana a Senai, zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi limodzi kudza makumi atatu.
36. Ansembe: ana a Yedaya, a nyumba ya Yesuwa, mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu ndi awiri kudza atatu.
37. Ana a lmneri, cikwi cimodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.
38. Ana a Pasuru, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi anai ndi asanu ndi awiri.