Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 2:19-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ana a Hasumu, mazana awiri mphambu makumi awiri kudza atatu.

20. Ana a Gibara, makumi asanu ndi anai mphambu asanu.

21. Ana a Betelehemu zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.

22. Anthu a ku Netofa, makumi asanu mphambu asanu ndi mmodzi.

23. Anthu a ku Anatoti, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.

24. Ana a Azimaveti, makumi anai mphambu awiri.

25. Ana a Kiriyati Arimu, Kefira, ndi Beeroti, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi anai kudza atatu.

26. Ana a Rama ndi Gaba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.

27. Anthu a Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.

28. Anthu a ku Beteli ndi Ai, mazana awiri mphambu makumi awiri kudza atatu.

29. Ana a Nebo, makumi asanu mphambu awiri.

30. Ana a Magabisi, zana limodzi mphambu makumi asanu kudza asanu ndi mmodzi.

31. Ana a Elamu wina, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi asanu ndi anai.

32. Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.

33. Ana a Lodi, Hadidi, ndi Ono, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi awiri kudza asanu.

34. Ana a Yeriko, mazana atatu mphambu makumi anai kudza asanu.

35. Ana a Senai, zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi limodzi kudza makumi atatu.

36. Ansembe: ana a Yedaya, a nyumba ya Yesuwa, mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu ndi awiri kudza atatu.

Werengani mutu wathunthu Ezara 2