17. Ana a Bezai, mazana atatu mphambu makumi awiri kudza atatu.
18. Ana a Yora, zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.
19. Ana a Hasumu, mazana awiri mphambu makumi awiri kudza atatu.
20. Ana a Gibara, makumi asanu ndi anai mphambu asanu.
21. Ana a Betelehemu zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.
22. Anthu a ku Netofa, makumi asanu mphambu asanu ndi mmodzi.
23. Anthu a ku Anatoti, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.
24. Ana a Azimaveti, makumi anai mphambu awiri.
25. Ana a Kiriyati Arimu, Kefira, ndi Beeroti, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi anai kudza atatu.
26. Ana a Rama ndi Gaba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.
27. Anthu a Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.
28. Anthu a ku Beteli ndi Ai, mazana awiri mphambu makumi awiri kudza atatu.
29. Ana a Nebo, makumi asanu mphambu awiri.
30. Ana a Magabisi, zana limodzi mphambu makumi asanu kudza asanu ndi mmodzi.
31. Ana a Elamu wina, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi asanu ndi anai.
32. Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.