Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 2:1-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ana a deralo, amene anakwera kuturuka m'ndende mwa andende aja Nebukadinezara mfumu ya Babulo adawatenga ndende kumka nao ku Babulo, nabwerera kumka ku Yerusalemu ndi Yuda, yense ku mudzi wace, ndi awa:

2. ndiwo amene adadza ndi Zerubabele, Yesuwa, Nehemiya, Seraya, Reelaya, Moredekai, Bilisani, Misipara, Bigivai, Rehumu, Baana. Kuwerenga kwa amuna a anthu a Israyeli ndiko:

3. ana a Parosi, zikwi ziwiri ndi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.

4. Ana a Sefatiya, mazana atatu mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.

5. Ana a Ara, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi asanu ndi awiri kudza asanu.

6. Ana a Pahati Moabu, a ana a Yesuwa ndi Yoabu, zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi atatu kudza khumi ndi awiri.

7. Ana a Elamu, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi asanu ndi anai.

8. Ana a Zatu, mazana asanu ndi anai mphambu makumi anai kudza asanu.

9. Ana a Zakai, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi asanu ndi limodzi.

10. Ana a Bani, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi anai kudza awiri.

11. Ana a Bebai, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.

12. Ana a Asigadi, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi awiri ndi awiri.

13. Ana a Adonikamu, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi mmodzi.

14. Ana a Bigivai, zikwi ziwiri mphambu makumi asanu kudza asanu ndi mmodzi.

15. Ana a Adini, mazana anai mphambu makumi asanu kudza anai.

16. Ana a Ateri, a Hezekiya, makumi asanu ndi anai mphambu asanu ndi atatu.

Werengani mutu wathunthu Ezara 2