Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 40:9-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Pamenepo ukatenge mafuta odzoza, ndi kudzoza nao kacisi, ndi zonse ziri m'mwemo, ndi kumpatula, ndi zipangizo zace zonse; ndipo adzakhala wopatulika.

10. Ndipo udzoze guwa la nsembe yopsereza, ndi zipangizo zace zonse, ndi kulipatula guwalo; ndipo guwalo lidzakhala lopatulikitsa.

11. Udzozenso mkhate ndi tsinde lace, ndi kuupatula.

12. Ndipo ubwere nao Aroni ndi ana ace amuna ku khomo la cihema cokomanako, ndi kuwasambitsa ndi madzi.

13. Nubveke Aroni cobvala zopatulikazo; ndi kumdzoza, ndi kumpatwa andicitire Ine nchito ya nsembe.

14. Ndipo ubwere nao ana ace amuna ndi kuwabveka maraya am'kati;

15. nuwadzoze, monga unadzoza atate wao, kuti andicitire nchito ya nsembe; ndi kudzozedwa kwao kuwakhalire unsembe wosatha mwa mibadwo yao.

16. Anatero Mose; monga mwa zonse Yehova adamuuza, momwemo anacita.

17. Ndipo kunali, mwezi woyamba wa caka caciwiri, tsiku loyamba la mwezi, anautsa kacisi.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 40