Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 40:6-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo ukaike guwa la nsembe yopsereza kunja kwa khomo la kacisi wa cihema cokomanako.

7. Ukaikenso mkhate pakati pa cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe, ndi kuthiramo madzi.

8. Ndipo ukamange mpandawo pozungulira, ndi kupacika nsaru yotsekera pa cipata ca pabwalo.

9. Pamenepo ukatenge mafuta odzoza, ndi kudzoza nao kacisi, ndi zonse ziri m'mwemo, ndi kumpatula, ndi zipangizo zace zonse; ndipo adzakhala wopatulika.

10. Ndipo udzoze guwa la nsembe yopsereza, ndi zipangizo zace zonse, ndi kulipatula guwalo; ndipo guwalo lidzakhala lopatulikitsa.

11. Udzozenso mkhate ndi tsinde lace, ndi kuupatula.

12. Ndipo ubwere nao Aroni ndi ana ace amuna ku khomo la cihema cokomanako, ndi kuwasambitsa ndi madzi.

13. Nubveke Aroni cobvala zopatulikazo; ndi kumdzoza, ndi kumpatwa andicitire Ine nchito ya nsembe.

14. Ndipo ubwere nao ana ace amuna ndi kuwabveka maraya am'kati;

15. nuwadzoze, monga unadzoza atate wao, kuti andicitire nchito ya nsembe; ndi kudzozedwa kwao kuwakhalire unsembe wosatha mwa mibadwo yao.

16. Anatero Mose; monga mwa zonse Yehova adamuuza, momwemo anacita.

17. Ndipo kunali, mwezi woyamba wa caka caciwiri, tsiku loyamba la mwezi, anautsa kacisi.

18. Ndipo Mose anautsa kacisi, nakhazika makamwa ace, naimika matabwa ace, namangapo mitanda yace, nautsa mizati ndi nsanamira zace.

19. Ndipo anayalika hema pamwamba pa kacisi, naika cophimba ca cihema pamwamba pace; monga Yehova adamuuza Mose.

20. Ndipo anatenga mboniyo, naiika mlikasa, napisa mphiko palikasa, naika cotetezerapo pamwamba pa likasa;

21. nalowa nalo likasa m'kacisi, napacika nsaru yocinga, nacinga likasa la mboni; monga Yehova adamuuza Mose.

22. Ndipo anaika gomelo m'cihema cokomanako, pa mbali ya kumpoto ya kacisi, kunja kwa nsaru yocinga.

23. Nakonzerapo mkate pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

24. Ndipo anaika coikapo nyali m'cihema cokomanako, popenyana ndi gome, pa mbali ya kumwela ya kacisi.

25. Nayatsa nyalizo pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 40