Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 40:23-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Nakonzerapo mkate pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

24. Ndipo anaika coikapo nyali m'cihema cokomanako, popenyana ndi gome, pa mbali ya kumwela ya kacisi.

25. Nayatsa nyalizo pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

26. Ndipo anaika guwa la nsembe lagolidi m'cihema cokomanako cakuno ca nsaru yocinga;

27. nafukizapo cofukiza ca pfungo lokoma; monga Yehova adamuuza Mose.

28. Ndipo anapacika kukacisi nsaru yotsekera pakhomo.

29. Ndipo anaika guwa la nsembe yopsereza pa khomo la kacisi wa cihema cokomanako, natenthapo nsembe yopsereza, ndi nsembe yaufa; monga Yehova adamuuza Mose.

30. Ndipo anaika mkhate pakati pa cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe; nathiramo madzi osamba.

31. Ndipo Mose ndi Aroni ndi ana ace amuna anasamba manja ao ndi mapazi ao m'menemo;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 40