19. Ndipo anayalika hema pamwamba pa kacisi, naika cophimba ca cihema pamwamba pace; monga Yehova adamuuza Mose.
20. Ndipo anatenga mboniyo, naiika mlikasa, napisa mphiko palikasa, naika cotetezerapo pamwamba pa likasa;
21. nalowa nalo likasa m'kacisi, napacika nsaru yocinga, nacinga likasa la mboni; monga Yehova adamuuza Mose.
22. Ndipo anaika gomelo m'cihema cokomanako, pa mbali ya kumpoto ya kacisi, kunja kwa nsaru yocinga.
23. Nakonzerapo mkate pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.
24. Ndipo anaika coikapo nyali m'cihema cokomanako, popenyana ndi gome, pa mbali ya kumwela ya kacisi.
25. Nayatsa nyalizo pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.
26. Ndipo anaika guwa la nsembe lagolidi m'cihema cokomanako cakuno ca nsaru yocinga;
27. nafukizapo cofukiza ca pfungo lokoma; monga Yehova adamuuza Mose.
28. Ndipo anapacika kukacisi nsaru yotsekera pakhomo.