Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 40:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2. Tsiku loyamba la mwezi woyamba ukautse kacisi wa cihema cokomanako.

3. Ndipo ukaikemo likasa la mboni, nucinge likasalo ndi nsaru yocingayo.

4. Ulongenso gomelo, nukonzerepo zokonzera zace; ulongenso coikapo nyalico, ndi kuyatsa nyali zace.

5. Ndipo ukaike guwa la nsembe lofukizapo lazolidi cakuno ca likasa la mboni, numange pakacisi nsaru yotsekera pakhomo.

6. Ndipo ukaike guwa la nsembe yopsereza kunja kwa khomo la kacisi wa cihema cokomanako.

7. Ukaikenso mkhate pakati pa cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe, ndi kuthiramo madzi.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 40