Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 4:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Mose anayankha nati, Koma taonani, sadzakhulupirira ine, kapena kumvera mau anga; pakuti adzanena, Yehova sanakuonekera iwe.

2. Ndipo Yehova ananena naye, Ico nciani m'dzanja lako? Nati, Ndodo.

3. Ndipo ananena iye, Iponye pansi. Naiponya pansi, ndipo inasanduka njoka; ndipo Mose anaithawa.

4. Koma Yehova anati kwa Mose, Tambasula dzanja lako, nuigwire kumcira; ndipo anatambasula dzanja lace, naigwira, nikhalanso ndodo m'dzanja lace;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 4