Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 39:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo anaiika pa zapamapewa za efodi, ikhale miyala ya cikumbutso kwa ana a Israyeli; monga Yehova adamuuza Mose.

8. Ndipo anaomba capacifuwa, nchito ya mmisiri, monga maombedwe ace a efodi; ca golidi, lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

9. Cinakhala camowamphwa; anaciomba capacifuwa copindika; utali wace cikhato cimodzi, ndi kupingasa kwace cikhato cimodzi, cinakhala copindika.

10. Ndipo anaika pomwepo mizere inai ya miyala; mzere wa odemu, pitida, ndi bareketi, ndiyo ya mzere woyamba.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 39