Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 38:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo anayengera mathungo anai a made amkuwawo mphete zinai, zikhale zopisamo mphiko.

6. Napanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndi mkuwa.

7. Ndipo anapisa mphikozo m'zimphetemo pa mbali za guwa la nsembe, kulinyamulira nazo; analipanga ndi matabwa, lagweregwere.

8. Ndipo anapanga mkhate wamkuwa, ndi tsinde lace lamkuwa, wa akalirole a akazi otumikira, akutumikira pa khomo la cihema cokomanako.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 38