Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 37:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Mphetezo zinali pafupi pa mitanda, zikhale zopisamo mphiko kunyamulira nazo gomelo.

15. Ndipo anapanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndigolidi, kunyamulira nazo gomelo.

16. Anapanganso zipangizo za gomelo, mbale zace, ndi zipande zace, ndi mitsuko yace, ndi zikho zace zakuthira nazo, za golidi woona.

17. Ndipo anapanga coikapo nyali ca golidi woona; mapangidwe ace a coikapo nyalico anacita cosula, tsinde lace ndi thupi lace, zikho zace, mitu yace, ndi maluwa ace zinakhala zocokera m'mwemo;

18. ndi m'mbali zace munaturuka mphanda zisanu ndi imodzi; mphanda zitatu za coikapo nyali zoturuka m'mbali yace imodzi, ndi mphanda zitatu za coikapo nyali zoturuka m'mbali yace yina;

19. pa mphanda imodzi panali zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi luwa; ndi pa mphanda yina zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi luwa; zinatero mphanda zisanu ndi imodzi zoturuka m'coikapo nyali.

20. Ndipo pa coikapo nyali comwe panali zikho zinai zopangika ngati katungurume, mitu yace ndi maluwa ace;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 37