Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 37:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo analiyengera mphete zinai zagolidi, naika mphetezo pa ngondya zace zinai zokhala pa miyendo yace inai.

14. Mphetezo zinali pafupi pa mitanda, zikhale zopisamo mphiko kunyamulira nazo gomelo.

15. Ndipo anapanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndigolidi, kunyamulira nazo gomelo.

16. Anapanganso zipangizo za gomelo, mbale zace, ndi zipande zace, ndi mitsuko yace, ndi zikho zace zakuthira nazo, za golidi woona.

17. Ndipo anapanga coikapo nyali ca golidi woona; mapangidwe ace a coikapo nyalico anacita cosula, tsinde lace ndi thupi lace, zikho zace, mitu yace, ndi maluwa ace zinakhala zocokera m'mwemo;

18. ndi m'mbali zace munaturuka mphanda zisanu ndi imodzi; mphanda zitatu za coikapo nyali zoturuka m'mbali yace imodzi, ndi mphanda zitatu za coikapo nyali zoturuka m'mbali yace yina;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 37