Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 36:36-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Ndipo anaipangira mizati inai yasitimu, nazikuta ndi golidi; zokowera zao zinali zagolidi; ndipo anaziyengera makamwa anai asiliva.

37. Ndipo anaomba nsaru yotsekera pa khomo la cihemaco, ya lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, nchito ya wopikula;

38. ndi nsamamira zace zisanu ndi zokowera zao; nakuta mitu yao ndi mitanda yao ndi golidi; ndi makamwa ao asanu anali amkuwa.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 36