Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 36:29-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Ndipo anaphatikizika pamodzi patsinde, naphatikizilca pamodzi pamutu pace ndi mphete imodzi; anatero nao onse awiri pa ngondya ziwiri.

30. Ndipo panali matabwa asanu ndi atatu ndi makamwa ao asiliva, makamwa khumi kudza asanu ndi limodzi; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi.

31. Ndipo anapanga mitanda ya mtengo wasmmu; Isanu ya matabwa a pa mbali yina ya kacisi,

32. ndi mitanda isanu ya matabwa a pa mbali inzace ya kacisi, ndi mitanda lsanu ya matabwa a kacisi ali pa mbali ya kumadzulo.

33. Ndipo anapititsa mtanda wa pakatipo, pakati pa matabwa kufikira kuthungo.

34. Ndipo anakuta matabwa ndi golidi, napanga mphete zao zagolidi zikhale zopisamo mitandayo, nakuta mitandayo ndi golidi.

35. Ndipo anaomba nsaru yocinga ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa; anaciomba ndi akerubi nchito ya mmisiri.

36. Ndipo anaipangira mizati inai yasitimu, nazikuta ndi golidi; zokowera zao zinali zagolidi; ndipo anaziyengera makamwa anai asiliva.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 36