Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 36:27-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndi ku mbali ya kumbuyo ya kacisi kumadzulo anapanga matabwa asanu ndi limodzi.

28. Anapanganso matabwa awiri a ku ngondya za kacisi, m'mbali zace ziwirio

29. Ndipo anaphatikizika pamodzi patsinde, naphatikizilca pamodzi pamutu pace ndi mphete imodzi; anatero nao onse awiri pa ngondya ziwiri.

30. Ndipo panali matabwa asanu ndi atatu ndi makamwa ao asiliva, makamwa khumi kudza asanu ndi limodzi; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi.

31. Ndipo anapanga mitanda ya mtengo wasmmu; Isanu ya matabwa a pa mbali yina ya kacisi,

32. ndi mitanda isanu ya matabwa a pa mbali inzace ya kacisi, ndi mitanda lsanu ya matabwa a kacisi ali pa mbali ya kumadzulo.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 36