6. golidi, ndi siliva, ndi mkuwa; ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;
7. ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wasitimu;
8. ndi mafuta akuunikira, ndi zonunkhira za mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma;
9. ndi miyala yasohamu, ndi miyala yoika ya efodi, ndi ya capacifuwa.
10. Ndipo abwere yense wa mtima waluso mwa inu, napange zonse zimene Yehova anauza;
11. kacisi, hema wace, ndi cophimba cace, zokowera zace, ndi matabwa ace, mitanda yace, mizati, nsanamira, ndi nsici zace, ndi makamwa ao;
12. likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;
13. gome, ndi mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;
14. ndi coikapo nyali ca kuunika, ndi zipangizo zace, ndi nyali zace, ndi mafuta a kuunika;
15. ndi guwa la nsembe lofukizapo, ndi mphiko zace, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsaru yotsekera pakhomo, pa khomo la kacisi;
16. guwa la nsembe yopereza, ndi made amkuwa, mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, mkhate ndi tsinde lace;
17. nsaru zocingira za kubwalo, nsici zace, ndi makamwa ace, ndi nsaru yotsekera ku cipata ca pabwalo;
18. ziciri za cihema, ndi ziciri za kubwalo, ndi zingwe zao;
19. zobvala za kutumikira nazo m'maopatulika, zobvala zopatulika za. Aroni wansembe, ndi zobvala za ana ace, zakugwira nazo nchito ya nsembe.