Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 35:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Mumtengere Yehova copereka ca mwa zanu; ali yense wa mtima womfunitsa mwini abwere naco, ndico copereka ca Yehova;

6. golidi, ndi siliva, ndi mkuwa; ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;

7. ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wasitimu;

8. ndi mafuta akuunikira, ndi zonunkhira za mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma;

9. ndi miyala yasohamu, ndi miyala yoika ya efodi, ndi ya capacifuwa.

10. Ndipo abwere yense wa mtima waluso mwa inu, napange zonse zimene Yehova anauza;

11. kacisi, hema wace, ndi cophimba cace, zokowera zace, ndi matabwa ace, mitanda yace, mizati, nsanamira, ndi nsici zace, ndi makamwa ao;

12. likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 35