Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 35:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;

13. gome, ndi mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;

14. ndi coikapo nyali ca kuunika, ndi zipangizo zace, ndi nyali zace, ndi mafuta a kuunika;

15. ndi guwa la nsembe lofukizapo, ndi mphiko zace, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsaru yotsekera pakhomo, pa khomo la kacisi;

16. guwa la nsembe yopereza, ndi made amkuwa, mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, mkhate ndi tsinde lace;

17. nsaru zocingira za kubwalo, nsici zace, ndi makamwa ace, ndi nsaru yotsekera ku cipata ca pabwalo;

18. ziciri za cihema, ndi ziciri za kubwalo, ndi zingwe zao;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 35