12. likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;
13. gome, ndi mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;
14. ndi coikapo nyali ca kuunika, ndi zipangizo zace, ndi nyali zace, ndi mafuta a kuunika;
15. ndi guwa la nsembe lofukizapo, ndi mphiko zace, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsaru yotsekera pakhomo, pa khomo la kacisi;
16. guwa la nsembe yopereza, ndi made amkuwa, mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, mkhate ndi tsinde lace;
17. nsaru zocingira za kubwalo, nsici zace, ndi makamwa ace, ndi nsaru yotsekera ku cipata ca pabwalo;
18. ziciri za cihema, ndi ziciri za kubwalo, ndi zingwe zao;