Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 35:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo abwere yense wa mtima waluso mwa inu, napange zonse zimene Yehova anauza;

11. kacisi, hema wace, ndi cophimba cace, zokowera zace, ndi matabwa ace, mitanda yace, mizati, nsanamira, ndi nsici zace, ndi makamwa ao;

12. likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;

13. gome, ndi mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;

14. ndi coikapo nyali ca kuunika, ndi zipangizo zace, ndi nyali zace, ndi mafuta a kuunika;

15. ndi guwa la nsembe lofukizapo, ndi mphiko zace, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsaru yotsekera pakhomo, pa khomo la kacisi;

16. guwa la nsembe yopereza, ndi made amkuwa, mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, mkhate ndi tsinde lace;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 35